04/08/2026
PETER MPONDA WAMUNG'ALULA CHIGOGA
Malingana ndi Mphunzitsi wakale watimu ya FCB Nyasa Big Bullets Peter Mponda wati zinthu zingapo zimaoneka ngati zikumuvuta ali k*timuyi chifukwa choti mkulu wa adindo k*timuyi Albert Chigoga sankamufuna k*timuyi in short anali galu ndi fisi.
Iye amayankhula pa pulogalamu ya Wa Ganyu Exclusive lachiwiri pomwe anali kufotokoza umoyo wake mu uphunzitsi.
Iye wati atapita ku Bullets, osewera ochuluka omwe ankadalilika anachoka komabe sanagulilidwe osewera omwe amawafuna.
"Tinapempha za Masiya Manda koma zinakanika kenako tinamvana ndi Chitipa United k*ti titenge Andrew Joseph koma zinakanidwa mpake tinayamba k*tenga osewera omwe alibe mgwirizano ndi timu iliyonse," anatero Mponda.
Iye wati kuchotsedwa kwake k*timuyi linali phuma kamba koti zina zomwe zinali mu mgwirizano wake sanaziyang'anire ndipotu kalata inamupeza ali mu bus.
Mponda wayankhulanso zokhudza Khuda Muyaba k*ti osewerayu ati sanakondwe ndi k*tulutsidwa pa masewero awo ndi Mighty Wanderers pomwe ankati iye si osewera otuluka pakati pa masewero.
Iye watinso timu yake ya Masters FC yaika mulingo wotenga ligi ya FDH Premiership kapena mu matimu anayi oyamba mu ligiyi.
kumpira ku eeee kuli ndale zoopsa
Ndipo lero Gangata anakumana ndi Khuda komaso osewera ena kuwauza zoti azinvera coach ndipo ngt yemwe sakufuna timui achoke ndipo Khuda anavomera k*ti achoka ndipo Gangata wamuuza k*ti abweze K10million yake ya signing on Fee yomwe Khuda anapochela
awa akufunika ku mental iyiyi ndimisala