08/01/2026
WOSEWERA MPIRA WA TIMU YA ALGERIA MOHAMED AMOURA WAPEPETSA
Mohamed Amoura wapepetsa kwa ochemelera wa timu ya dziko la D.R Congo pomwe anayerekezera momwe ochemelera wa timu ya Congo amapanga poimilira, osegwedela ndikuimika dzanja m'mwamba pa masewero onse a timu ya Congo ndipo izi zimaimila, Patrice Lumumba chizindikiro chosonyeza kuziimila paokha kwa dziko la DRC, kuchoka muokapolo, kukhala ozilamulira okha.
M'mawu ake Amoura wati masewero omwe amasewera ndi Congo anali masewero akulu, opatsa ntheng'eneng'e m'bwalo lazamasewero.
Ndikufuna anthu andimvetsetse panthawi yomwe ndimayesezera Lumumba sindimaziwa zomwe zimatanthauza, ndinangopanga mwansangulutso chabe ndinalibe lingaliro lilironse lonyoza kapena kufuna kuyambitsa kusamvana.
Ndimalemekeza timu ya Congo ndipo ndikuifunira zabwino zonse pomwe ikukapikitsana nawo pa masewero ofuna kuzigulira malo ku mpikisano wa pa dziko lonse omwe uchitikire ku maiko a America, Mexico ndi Canada.
Ngati kachitidwe kanga kanali kosokoneza ndikupepetsa chifukwa sichinali chikonzero changa.
Timu ya Algeria inagonjetsa D.R Congo ndichigoli chimodzi kwa duu chomwe chinabwera mu mphindi 90 ndi 29 zowonjedzera mwapadeladela.